
Kuyimba ku ma gulu a anthu ndi ma ulendo
3. Kuyimba ku ma gulu a anthu ndi ma ulendo
Ma ulendo a mu dziko mwathu ndi a kunja kwa dziko
Anthu oyimba akhoza kulinganiza ma ulendo mu dziko la Malawi komanso atha kusaka mwayi okawonetsa luso lawo ku mayiko amene tayandikana nawo. Kuwonetsera luso lawo ku ma gulu a wanthu, ku malo osangalalila kapenanso kuzilinganizo zina kukhoza kubweretsa phindu la ndalama zochuluka.
Kuchemerera ndi kuyitanidwa
Kuwonetsera luso kumagulu kopambana kumafunika kuyitanidwa ndi kuchemerera. Anthu oyimba atha kugwirizana ndi anthu olinganiza ndi kuchemerera kapena kuyitanira kuti athe kufikira omvera ambiri komanso kuwonetsetsa kuti ku zilinganizo zawo kwabwera anthu ochuluka.